Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. umenenso mupulumutsidwa nao ngati muugwiritsa monga momwe ndinalalikira kwa inu; ngati simunakhulupira cabe.

3. Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, cimenenso ndinalandira, kuti Kristuanafera zoipa zathu, mongamwa malembo;

4. ndi kuti anaikidwa; ndi kutianaukitsidwa tsiku lacitatu, monga mwa malembo;

5. ndi kuti anaonekera kwa Kefa; pamenepo kwa khumi ndi awiriwo;

6. pomwepo anaoneka pa nthawi imodzi kwa abale oposa mazana asanu, amene ocuruka a iwo akhala kufikira tsopano, koma ena agona;

7. pomwepoanaonekera kwa Yakobo; pamenepo kwa: atumwi onse;

8. ndipo potsiriza pace pa onse, anaoneka kwa inenso monga mtayo.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15