2. umenenso mupulumutsidwa nao ngati muugwiritsa monga momwe ndinalalikira kwa inu; ngati simunakhulupira cabe.
3. Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, cimenenso ndinalandira, kuti Kristuanafera zoipa zathu, mongamwa malembo;
4. ndi kuti anaikidwa; ndi kutianaukitsidwa tsiku lacitatu, monga mwa malembo;
5. ndi kuti anaonekera kwa Kefa; pamenepo kwa khumi ndi awiriwo;
6. pomwepo anaoneka pa nthawi imodzi kwa abale oposa mazana asanu, amene ocuruka a iwo akhala kufikira tsopano, koma ena agona;
7. pomwepoanaonekera kwa Yakobo; pamenepo kwa: atumwi onse;
8. ndipo potsiriza pace pa onse, anaoneka kwa inenso monga mtayo.