Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma ngati kulibe kuuka kwa akufa, Kristunso sanaukitsidwa;

14. ndipo ngati Kristu sanaukitsidwakulalikira kwathu kuli cabe, cikhulupiriro canunso ciri cabe.

15. Ndiponso ife tipezedwa mboni zonama za Mulungu; cifukwa n tinacita umboni kunena za Mulungu kuti anaukitsa Kristu; amene sanamuukitsa, ngati kuli tero kuti akufa saukitsidwa,

16. Pakuti ngati akufa saukitsidwa, Kristunso sanaukitsidwa;

17. ndipo ngati Kristu sanaukitsidwa, cikhulupiriro canu ciri copanda pace; muli cikhalire m'macimo anu.

18. Cifukwa cace iwonso akugona mwa Kristu anatayika.

19. Ngati tiyembekezera Kristu m'moyo uno wokha, tiri ife aumphawi oposa a anthu onse,

20. Koma tsopano Kristu waukitsidwa kwa akufa, cipatso coundukula ca iwo akugona.

21. Pakuti monga imfa inadza mwa munthu, kuuka kwa akufa kunadzanso mwa munthu.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15