Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:12-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma ngati Kristu alalikidwa kuti waukitsidwa kwa akufa, nanga ena mwa inu anena bwanjikuti kulibe kuuka kwa akufa?

13. Koma ngati kulibe kuuka kwa akufa, Kristunso sanaukitsidwa;

14. ndipo ngati Kristu sanaukitsidwakulalikira kwathu kuli cabe, cikhulupiriro canunso ciri cabe.

15. Ndiponso ife tipezedwa mboni zonama za Mulungu; cifukwa n tinacita umboni kunena za Mulungu kuti anaukitsa Kristu; amene sanamuukitsa, ngati kuli tero kuti akufa saukitsidwa,

16. Pakuti ngati akufa saukitsidwa, Kristunso sanaukitsidwa;

17. ndipo ngati Kristu sanaukitsidwa, cikhulupiriro canu ciri copanda pace; muli cikhalire m'macimo anu.

18. Cifukwa cace iwonso akugona mwa Kristu anatayika.

19. Ngati tiyembekezera Kristu m'moyo uno wokha, tiri ife aumphawi oposa a anthu onse,

20. Koma tsopano Kristu waukitsidwa kwa akufa, cipatso coundukula ca iwo akugona.

21. Pakuti monga imfa inadza mwa munthu, kuuka kwa akufa kunadzanso mwa munthu.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15