Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 15:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ndikudziwitsani, abale, Uthenga Wabwino umene ndinakulalikirani inu, umenenso munalandira, umenenso muimamo,

2. umenenso mupulumutsidwa nao ngati muugwiritsa monga momwe ndinalalikira kwa inu; ngati simunakhulupira cabe.

3. Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, cimenenso ndinalandira, kuti Kristuanafera zoipa zathu, mongamwa malembo;

4. ndi kuti anaikidwa; ndi kutianaukitsidwa tsiku lacitatu, monga mwa malembo;

5. ndi kuti anaonekera kwa Kefa; pamenepo kwa khumi ndi awiriwo;

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 15