Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 14:9-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Momwemonso inu ngati mwa lilime simupereka mau omveka bwino, kudzazindikirika bwanji cimene cilankhulidwa? Pakuti mudzakhala olankhula kumlengalenga.

10. Iripo, kaya, mitundu yambiri yotere ya mau pa dziko lapansi, ndipo palibe kanthu kasowa mau.

11. Cifukwa cace, ngati sindidziwa mphamvu ya mauwo ndidzakhala kwa iye wolankhulayo wakunja, ndipo wolankhulayo adzakhala wakunja kwaine.

12. Momwemo inunso, popeza muli ofunits its a mphatso zauzimu, funani kuti mukacuruke kukumangirira kwa Mpingo,

13. Cifukwa cace wolankhula lilime, apemphere kuti amasule.

14. Pakuti ngati ndipemphera m'lilime, mzimu wanga upemphera, koma cidziwitso canga cikhala cosabala kanthu.

15. Kuli ciani tsono? Ndidzapemphera ndi mzimu, koma ndidzapempheranso ndi cidziwitso canga; ndidzayimba ndi mzimu, koma ndidzayimbanso ndi cidziwitso.

16. Cifukwa ngati udalitsa ndi mzimu, nanga iye wakukhala wosaphunzira adzati Amen bwanji, pa kuyamika kwako, popeza sadziwa cimene unena?

17. Pakutitu iwe uyamika bwino, koma winayo samangiriridwa.

18. Ndiyanillca Mulungu kuti ndilankhula malilime koposa inu nonse;

19. koma mu Mpingo ndifuna kulankhula mau asanu ndi cidziwitso canga, kutinso ndikalangize ena, koposa kulankhula mau zikwi m'lilime.

20. Abale, musakhale ana m'cidziwitso, koma m'coipa khalani makanda, koma m'cidziwitso akulu misinkhu.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 14