Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 12:15-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ngati phazi likati, Popeza sindiri dzanja, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

16. Ndipo ngati khutu likati, Popeza sindiri diso, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

17. Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?

18. Koma tsopano, Mulungu anaika ziwalo zonsezo m'thupi, monga anafuna.

19. Koma ngati zonse zikadakhala ciwalo cimodzi, likadakhala kuti thupi?

20. Kama tsopano pali ziwalo zambiri, kama thupi limodzi.

21. Ndipo dise silingathe kunena kwa dzanja, Sindikufuna iwe, kapenanso mutu kwa mapazi, Sindikufunani inu.

22. Koma makamakatu ziwalozo zoyesedwa zofoka m'thupi, zifunika;

23. ndipo zimene tiziyesa Zocepa ulemum'thupi, pa izi tiika ulemu wocuruka woposa; ndi zinthu zosakoma zikhala naco cokometsera coposa,

24. Koma zokoma zathu ziribe kusowa; koma Mulungu analumikizitsa thupi, napatsa ulemu wocuruka kwa cosowaco; kuti kusakhale cisiyano m'thupi;

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 12