Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 12:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma za mphatso zauzimu, abale, sindifuna kuti mukhale osadziwa.

2. Mudziwa kuti pamene munali amitundu, munatengedwa kunka kwa mafano aja osalankhula, monga munatsogozedwa.

3. Cifukwa cace ndikuuzani inu, kuti palibe munthu wakulankhula mwa Mzimu wa Mulungu, anena, Yesu ngwotembereredwa; ndipo palibe wina akhoza kunena, Yew ali Ambuye, koma mwa Mzimu Woyera.

4. Ndipo pali mphatso zosiyana, koma Mzimu yemweyo.

5. Ndipo pali mautumiki osiyana, koma Ambuye yemweyo.

6. Ndipo pali macitidwe osiyana, koma Mulungu yemweyo, wakucita zinthu zonse mwa onse.

7. Koma kwa yense kwapatsidwa maonekedwe a Mzimu kuti apindule nao.

8. Pakuti kwa mmodzi kwapatsidwa mwa Mzimu mau a nzeru; koma kwa mnzace mau a cidziwitso, monga mwa Mzimu yemweyo:

9. kwa wina cikhulupiriro, mwa Mzimu yemweyo; ndi kwa wina mphatso za maciritso, mwa Mzimu mmodziyo;

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 12