Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 11:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma ngati mkazi aweta tsitsi, kuli ulemerero kwa iye; pakuti tsitsi lace lapatsidwa kwa iye ngati cophimba.

16. Koma akaoneka wina ngati wotetana, tiribe makhalidwe otere, kapena ife, kapena Eklesia wa Mulungu.

17. Koma pakulalikira ici sinditama inu, popeza simusonkhanira cokoma, koma coipa.

18. Pakutitu poyamba posonkhana inu mu Mpingo, ndimva kuti pakhala malekano mwa inu; ndipo ndibvomereza penapo.

19. Pakuti kuyenera kuti pakhale mipatuko mwa inu, kuti iwo obvomerezedwa aonetsedwemwa inu.

20. Cifukwa cace, pakusonkhana inu pamodzi sikutheka kudya mgonero wa Ambuye;

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 11