5. Koma ocuruka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'cipululu.
6. Koma zinthu izi zinacitika, zikhale zoticenjeza ife, kuti tisalakalake zoipa ife, monganso iwowo analakalaka.
7. Kapena musakhale opembedza mafano, monga ena a iwo, monga kwalembedwa, Anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nanyamuka kusewera.
8. Kapena tisacite dama monga ena a iwo anacita dama, nagwa tsiku limodzi zikwi makumi awiri ndi zitatu.
9. Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija.