Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 10:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndinena cikumbu mtima, si ca iwe mwini, koma ca winayo; 1 pakuti ufulu wanga uyesedwa ninji ndi cikumbu mtima ca wina?

30. Ngati ine ndilandirako mwacisomo, ndinenezedwa bwanji cifukwa ca ici cimene ndiyamikapo?

31. Cifukwa cace 2 mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale mucita kanthu kena, citani zonse ku ulemerero wa Mulungu.

32. 3 Khalani osakhumudwitsa, kapena Ayuda, kapena Ahelene, kapena Mpingo wa Mulungu;

33. monga 4 inenso ndikodweretsa onse m'zinthu zonse, wosafuna cipindulo canga, koma ca unyinjiwo, kuti apulumutsidwe.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 10