Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 10:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti sindifuna, kuti mukhale osadziwa, abale, kuti makolo athu onse anali pansi pa mtambo, naoloka nyanja onse;

2. nabatizidwa onse kwa Mose, mumtambo, ndi m'nyanja,

3. nadya onse cakudya cauzimu cimodzimodzi;

4. namwa onse cakumwa cauzimu cimodzimodzi; pakuti anamwa mwa thanthwe lauzimu lakuwatsata; koma thanthwelo ndiye Kristu.

5. Koma ocuruka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'cipululu.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 10