Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 1:5-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. kuti m'zonse muoalemezedwa mwa iye, m'mau onse, ndi cidziwitso conse;

6. mongaumboni wa Kristu unakhazikika mwa inu;

7. kotero kuti sicikusowani inu caufuru ciri conse; pakulindira inu bvumbulutso la Ambuye wathu Yesu Kristu;

8. amenenso adzakukhazikitsani inu kufikira cimariziro, kuti mukhale opanda cifukwa m'tsiku la Ambuye: wathu Yesu Kristu.

9. Mulungu ali, wokhulupirika amene munaitanidwa mwa iye, ku ciyanjano ca Mwana wace Yesu Kristu, Ambuye wathu.

10. Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu, kuti munene cimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m'ciweruziro comweco.

11. Pakuti zinamveka kwa ine za inu, abale anga, ndi iwo a kwa Kloe, kuti pali makani pakati pa inu.

12. Koma ici ndinena, kuti yense wa inu anena, Ine ndine wa Paulo; koma ine wa Apolo; koma ine wa Kefa; koma ine wa Kristu.

13. Kodi Kristu wagawika? Kodi Paulo anapacikidwa cifukwa ca inu? Kapena kodi munabatizidwa m'dzina la Paulo?

14. Ndiyamika Mulungu kuti sindinabatiza mmodzi yense wa inu, koma Krisipo ndi Gayo;

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 1