Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 7:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Zekariya, ndi kuti,

9. Watero Yehova wa makamu, kuti, Weruzani ciweruzo coona, nimucitire yense mnzace cifundo ndi ukoma mtima;

10. musazunza mkazi wamasiye, kapena ana amasiye, mlendo kapena waumphawi; ndipo nnena mmodzi wa inu alingirire m'mtima mwace kumcitira coipa munthu mnzace.

11. Koma anakana kumvera, nakaniza phewa lao, natseka makutu ao, kuti asamve.

12. Inde, anasanduliza mitima yao ikhale ngati mwala woti gwa, kuti angamve cilamulo, ndi mau amene Yehova wa makamu anatumiza ndi Mzimu wace mwa aneneri oyamba aja; m'menemo munafuma mkwiyo waukuru wocokera kwa Yehova wa makamu.

13. Ndipo kunacitika, monga Iye anapfuula, koma iwo sanamvera; momwemo iwo adzapfuula, koma Ine sindidzamva, ati Yehova wa makamu;

14. koma ndidzawabalalitsa ndi kabvumvulu mwa amitundu onse amene sanawadziwa. Motero dziko linakhala bwinja, m'mbuyo mwao; palibe munthu wopitapo ndi kubwererako; pakuti adaika dziko lofunikalo labwinja.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 7