Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zefaniya 1:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo ndidzatambasulira dzanja langa pa Yuda, ndi pa onse okhala m'Yerusalemu; ndipo a ndidzaononga otsala a Baala kuwacotsa m'malo muno, ndi dzina la Akemari pamodzi ndi ansembe;

5. ndi iwo akulambira khamu la kumwamba pamwamba pa matsindwi; ndi iwo akulambira, akulumbira pali Yehova, nalumbiranso pali mfumu;

6. ndi iwo akubwerera osamtsata Yehova; ndi osamfuna Yehova, kapena kufunsira kwa Iye.

7. Khala cete pamaso pa Ambuye Yehova; pakuti tsiku la Yehova liyandikira; pakuti Yehova wakonzeratu nsembe, anapatula oitanidwa ace.

8. Ndipo kudzacitika tsiku la nsembe ya Yehova, kuti ndidzalanga akalonga ndi ana a mfumu, ndi onse akubvala cobvala cacilendo.

9. Ndipo tsiku ilo ndidzalanga olumpha ciundo, nadzaza nyumba ya mbuye wao ndi ciwawa ndi cinyengo.

10. Ndipo tsiku ilo, ati Yehova, kudzakhala phokoso lakulira locokera ku cipata cansomba, ndi kucema kocokera ku dera laciwiri, ndi kugamuka kwakukuru kocokera kuzitunda.

11. Cemani okhala m'cigwa, pakuti amalonda onse atayika, onsewo osenza siliva aonongeka.

Werengani mutu wathunthu Zefaniya 1