Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zefaniya 1:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo tsiku ilo, ati Yehova, kudzakhala phokoso lakulira locokera ku cipata cansomba, ndi kucema kocokera ku dera laciwiri, ndi kugamuka kwakukuru kocokera kuzitunda.

11. Cemani okhala m'cigwa, pakuti amalonda onse atayika, onsewo osenza siliva aonongeka.

12. Ndipo kudzacitika nthawi yomweyi kuti ndidzasanthula Yerusalemu ndi nyali, ndipo ndidzalanga amunawo okhala ndi nsenga, onena m'mtima mwao, Yehova sacita cokoma, kapena kucita coipa.

13. Ndipo zolemera zao zidzakhala zakufunkhidwa; ndi nyumba zao zabwinja; adzamangadi nyumba, koma sadzagonamo; adzanka minda yampesa koma sadzamwa vinyo wace.

14. Tsiku lalikuru la Yehova liri pafupi, liri pafupi lifulumira kudza, mau a tsiku la Yehova; munthu wamphamvu adzalirapo mowawa mtima.

Werengani mutu wathunthu Zefaniya 1