Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoweli 3:13-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Longani zenga, pakuti dzinthu dzaca; idzani, pondani, pakuti cadzala coponderamo mphesa; zosungiramo zisefuka; pakuti zoipa zao nzazikuru.

14. Aunyinji, aunyinji m'cigwa cotsirizira mlandu! pakuti layandikira tsiku la Yehova m'cigwacotsiriziramlandu.

15. Dzuwa ndi mwezi zada, ndi nyenyezi zibweza kuwala kwao.

16. Ndipo Yehova adzadzuma ali ku Ziyoni, ndi kumveketsa mau ace ali ku Yerusalemu; ndi thambo ndi dziko lapansi zidzagwedezeka; koma Yehova adzakhala copulumukirako anthu ace, ndi linga la ana a Israyeli.

17. Momwemo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu wakukhala m'Ziyoni, phiri langa lopatulika; pamenepo Yerusalemu adzakhala wopatulika, osapitanso alendo pakati pace,

18. Ndipo kudzacitika tsiku ilo mapiri adzakhetsa vinyo wozuna, ndi pazitunda padzayenda mkaka, ndi m'mitsinje yonse ya Yuda mudzayenda madzi; ndi madzi a kasupe adzaturuka m'nyumba ya Yehova, nadzamwetsa madzi cigwa ca Sitimu.

19. Aigupto adzasanduka bwinja, ndi Edomu adzasanduka cipululu copanda kanthu, cifukwa ca ciwawaci anawacitira ana a Yuda; popeza anakhetsa mwazi wosacimwa m'dziko lao.

20. Koma Yuda adzakhala cikhalire, ndi Yerusalemu ku mibadwo mibadwo.

21. Ndipo ndidzayeretsa mwazi wao umene sindinauyeretsa, pakuti Yehova akhala m'Ziyoni.

Werengani mutu wathunthu Yoweli 3