Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoweli 2:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pamaso pao mitundu ya anthu ikumva zowawa, nkhope zonse zitumbuluka.

7. Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda liri lonse njira yace, osasokonezeka m'mabande ao.

8. Sakankhana, ayenda liri lonse m'mopita mwace; akagwa m'zida, siityoka nkhondo yao.

9. Alumphira mudzi, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati mkhungu.

10. Dziko lapansi linjenjemera pamaso pao, thambo ligwedezeka, dzuwa ndi mwezi zada, ndi nyenyezi zi'bweza kuwala kwao;

Werengani mutu wathunthu Yoweli 2