Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoweli 2:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Muombe lipenga m'Ziyoni, nimupfuulitse m'phiri langa lopatulika; onse okhala m'dziko anjenjemere; pakuti tsiku la Yehova lirinkudza, pakuti liyandikira;

2. tsiku la mdima, la mdima wandiweyani, tsiku la mitambo, mitambo yocindikira, ngati m'mbandakuca moyalika pamapiri; mtundu waukuru ndi wamphamvu, panalibe wotere ndi kale lonse, sipadzakhalanso wotere utapita uwu, kufikira zaka za mibadwo yambiri.

3. Moto unyambita pamaso pao, ndi m'mbuyo mwao litentha lawi la moto; kumaso kwao dziko likunga munda wa Edeni, koma m'mbuyo mwao likunga cipululu copanda kanthu; palibenso wakuwapulumuka.

Werengani mutu wathunthu Yoweli 2