Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoweli 2:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Muombe lipenga m'Ziyoni, nimupfuulitse m'phiri langa lopatulika; onse okhala m'dziko anjenjemere; pakuti tsiku la Yehova lirinkudza, pakuti liyandikira;

2. tsiku la mdima, la mdima wandiweyani, tsiku la mitambo, mitambo yocindikira, ngati m'mbandakuca moyalika pamapiri; mtundu waukuru ndi wamphamvu, panalibe wotere ndi kale lonse, sipadzakhalanso wotere utapita uwu, kufikira zaka za mibadwo yambiri.

3. Moto unyambita pamaso pao, ndi m'mbuyo mwao litentha lawi la moto; kumaso kwao dziko likunga munda wa Edeni, koma m'mbuyo mwao likunga cipululu copanda kanthu; palibenso wakuwapulumuka.

4. Maonekedwe ao aoneka ngati akavalo, nathamanga ngati akavalo a nkhondo.

5. Atumphako ngati mkokomo wa magareta pamwamba pa mapiri, ngati kulilima kwa malawi a moto akupsereza ziputu, ngati mtundu wamphamvu wa anthu ondandalikira nkhondo.

6. Pamaso pao mitundu ya anthu ikumva zowawa, nkhope zonse zitumbuluka.

7. Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda liri lonse njira yace, osasokonezeka m'mabande ao.

8. Sakankhana, ayenda liri lonse m'mopita mwace; akagwa m'zida, siityoka nkhondo yao.

9. Alumphira mudzi, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati mkhungu.

10. Dziko lapansi linjenjemera pamaso pao, thambo ligwedezeka, dzuwa ndi mwezi zada, ndi nyenyezi zi'bweza kuwala kwao;

Werengani mutu wathunthu Yoweli 2