Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 4:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo kunali, atatha kuoloka anthu onse, likasa la Yehova linaoloka, ndi ansembe, pamaso pa anthu.

12. Ndipo ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi gawo lija la pfuko la Manase anaoloka ndi zida zao pamaso pa ana a Israyeli, monga Mose adanena nao;

13. ngati zikwi makumi anai ankhondo okonzeka anaoloka pamaso pa Yehova kuthira nkhondo ku zidikha za Yeriko.

14. Tsiku lomwelo Yehova anakulitsa Yoswa pamaso pa Aisrayeli onse; ndipo anamuopa monga anaopa Mose, masiku onse amoyowace.

15. Ndipo Yehova anati kwa Yoswa,

16. Lamulira ansembe akusenza likasa la umboni, kuti akwere kuturuka m'Yordano.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 4