1. Ndipo kunali, utatha kuoloka Yordano mtundu wonse, Yehova ananena ndi Yoswa, nati,
2. Mudzitengere mwa anthu, amuna khumi ndi awiri, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;
3. ndipo muwalamulire iwo ndi kuti, Mudzitengere pano pakati pa Yordano, poimapo mapazi a ansembe, miyala khumi ndi iwiri, ndi kuoloka nayo, ndi kulika m'mogona m'mene mugonamo usiku uno.