Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 21:9-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo anapatsa motapa pa pfuko la ana a Yuda, ndi pa pfuko la ana a Simeoni, midzi iyi yochulidwa maina ao;

10. kuti ikhale ya ana a Aroni a mabanja a Akohati, a ana a Levi, pakuti maere oyamba adaturukira iwowa.

11. Ndipo anawapatsa mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anoki, womwewo ndi Hebroni, ku mapiri a Yuda, ndi mabusa ace ozungulirapo.

12. Koma minda ya mudzi ndi miraga yace anapatsa Kalebe mwana wa Yefune, ikhale yace.

13. Ndipo kwa ana a Aroni wansembe anapatsa Hebroni ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzace, ndi Libina ndi mabusa ace;

14. ndi Yatiri ndi mabusa ace, ndi Esitimoa ndi mabusa ace;

15. ndi Holoni ndi mabusa ace, ndi Debiri ndi mabusa ace;

16. ndi Aini ndi mabusa ace, ndi Yuta ndi mabusa ace, ndi Betisemesi ndi mabusa ace; midzi isanu ndi inai yotapira mapfuko awiri aja.

17. Ndipo motapira pfuko La Benjamini, Gibeoni ndi mabusa ace, Geba ndi mabusa ace,

18. Anatotu ndi mabusa ace, ndi Alimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

19. Miclzi yonse ya ana a Aroni, ansembe, ndiyo khumi ndi itatu, ndi mabusa ao.

20. Ndipo mabanja a ana a Kohati, Aleviwo, otsala a ana a Kohati, analandira midzi ya maere ao motapira pa pfuko la Efraimu.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 21