Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 21:37-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Kedimotu ndi mabusa ace, ndi Mefati ndi mabusa ace; midzi inai.

38. Ndipo motapira m'pfuko la Gadi, Ramoti m'Gileadi ndi mabusa ace ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Mahanaimu ndi mabusa ace;

39. Hesiboni ndi mabusa ace. Yazeri ndi mabusa ace: yonse pamodzi midzi inai.

40. Yonseyi ndiyo midzi ya ana a Merari monga mwa mabanja ao, ndiwo otsala a mabanja a Alevi; ndipo gawo lao ndilo midzi khumi ndi iwiri.

41. Midzi yonse ya Alevi, pakati pa colowa ca ana a Israyeli ndiyo midzi makumi anai kudza isanu ndi itatu, ndi mabusa ao.

42. Midzi iyi yonse inali nao mabusa ao pozungulira pao: inatero midzi iyi yonse.

43. Motero Yehova anawapatsa Israyeli dziko lonse adalumbiralo kuwapatsa makolo ao: ndipo analilandira lao lao, nakhala m'mwemo.

44. Ndipo Yehova anawapatsa mpumulo pozungulira ponse, monga mwa zonse adalumbirira makolo ao; ndipo pamaso pao sipanaima munthu mmodzi wa adani ao onse; Yehova anapereka adani ao onse m'manja mwao.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 21