Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 21:2-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. nanena nao ku Silo m'dziko la Kanani, ndi kuti Yehova analamulira mwa dzanja la Mose kuti atipatse midzi yokhalamo ife, ndi mabusa a zoweta zathu.

3. Ndipo ana a Israyeli anapatsa Alevi, kutapa pa colowa cao, monga mwa lamulo la Yehova, midzi iyi ndi mabusa ao.

4. Ndipo maere anaturukira mabanja a Akohati; ndipo molota maere ana a Aroni wansembe, ndiwo Alevi, analandira motapa pa pfuko la Yuda, ndi pa pfuko la Simeoni, ndi pa pfuko la Benjamini, midzi khumi ndi itatu.

5. Ndipo ana otsala a Kohati analandira molota maere motapa pa mabanja a pfuko la Efraimu, ndi pa pfuko La Dani, ndi pa pfuko La Manase logawika pakati, midzi khumi.

6. Ndipo ana a Gerisoni analandira molota maere motapa pa mabanja a pfuko la Isakara, ndi pa pfuko la Aseri, ndi pa pfuko la Nafitali, ndi pa pfuko la Manase logawika pakati m'Basana, midzi khumi ndi itatu.

7. Ana a Merari, monga mwa mabanja ao, analandira motapa pa pfuko la Rubeni, ndi pa pfuko la Gadi, ndi pa pfuko la Zebuloni midzi khumi ndi iwiri.

8. Motero ana a Israyeli anapatsa Alevi midzi iyi ndi mabusa ao, molota maere, monga Yehova adalamulira mwa dzanja la Mose.

9. Ndipo anapatsa motapa pa pfuko la ana a Yuda, ndi pa pfuko la ana a Simeoni, midzi iyi yochulidwa maina ao;

10. kuti ikhale ya ana a Aroni a mabanja a Akohati, a ana a Levi, pakuti maere oyamba adaturukira iwowa.

11. Ndipo anawapatsa mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anoki, womwewo ndi Hebroni, ku mapiri a Yuda, ndi mabusa ace ozungulirapo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 21