Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 21:15-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ndi Holoni ndi mabusa ace, ndi Debiri ndi mabusa ace;

16. ndi Aini ndi mabusa ace, ndi Yuta ndi mabusa ace, ndi Betisemesi ndi mabusa ace; midzi isanu ndi inai yotapira mapfuko awiri aja.

17. Ndipo motapira pfuko La Benjamini, Gibeoni ndi mabusa ace, Geba ndi mabusa ace,

18. Anatotu ndi mabusa ace, ndi Alimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

19. Miclzi yonse ya ana a Aroni, ansembe, ndiyo khumi ndi itatu, ndi mabusa ao.

20. Ndipo mabanja a ana a Kohati, Aleviwo, otsala a ana a Kohati, analandira midzi ya maere ao motapira pa pfuko la Efraimu.

21. Ndipo anawapatsa Sekemu ndi mabusa ace ku mapiri a Efraimu, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Gezeri ndi mabusa ace;

22. ndi Kibizaimu ndi mabusa ace, Betihoroni ndi mabusa ace; midzi inai.

23. Ndipo motapira m'pfuko La Dani, Eliteke ndi mabusa ace, Gibetoni ndi mabusa ace;

24. Aijaloni ndi mabusa ace, Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

25. Ndipo motapira pa pfukola Manaselogawika pakati, Taanaki ndi mabusa ace, ndi Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi iwiri.

26. Midzi yonse ya mabanja a ana otsala a Kohati ndiyo khumi ndi mabusa ao.

27. Ndipo anapatsa ana a Gerisoni, a mabanja a Alevi, motapira pa pfuko la Manase logawika pakati, Golani m'Basana ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo; ndi Beesitera ndi mabusa ace; midzi iwiri.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 21