11. Ndipo anawapatsa mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anoki, womwewo ndi Hebroni, ku mapiri a Yuda, ndi mabusa ace ozungulirapo.
12. Koma minda ya mudzi ndi miraga yace anapatsa Kalebe mwana wa Yefune, ikhale yace.
13. Ndipo kwa ana a Aroni wansembe anapatsa Hebroni ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzace, ndi Libina ndi mabusa ace;
14. ndi Yatiri ndi mabusa ace, ndi Esitimoa ndi mabusa ace;
15. ndi Holoni ndi mabusa ace, ndi Debiri ndi mabusa ace;
16. ndi Aini ndi mabusa ace, ndi Yuta ndi mabusa ace, ndi Betisemesi ndi mabusa ace; midzi isanu ndi inai yotapira mapfuko awiri aja.