5. ndipo m'mene akadati atseke pacipata, kutada, anaturuka amunawo; uko anamuka amunawo osakudziwa ine; muwalondole msanga, pakuti mudzawapeza.
6. Koma adawakweretsa patsindwi, nawabisa ndi mitengo yanthamza yoyanika patsindwi.
7. Ndipo amunawo anawalondola pa njira ya ku Yordano yomka kudooko; ndipo ataturuka akuwalondola, anatseka pacipata.