Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 2:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Koma ukaulula codzera ifeco tidzamasukira lumbiro lako watilumbiritsali.

21. Nati iye, Momwemo, monga mwa mau anu. Ndipo anawauza amuke, iwo namuka; namanga iye cingwe cofiiraco pazenera.

22. Ndipo anayenda iwo, nafika kuphiri, nakhalako masiku atatu mpaka atabwerera olondolawo; popeza olondolawo anawafunafuna panjira ponse, osawapeza.

23. Pamenepo amuna awiriwo anabwerera, natsika m'phirimo naoloka, nafika kwa Yoswa mwana wa Nuni, namfotokozera zonse zidawagwera.

24. Ndipo anati kwa Yoswa, Zoonadi, Yehova wapereka dziko lonse m'manja mwathu; ndiponso nzika zonse zasungunuka pamaso pathu.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 2