Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 2:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo amunawo anati kwa iye, Sitidzacimwira lumbiro lako ili watilumbiritsali.

18. Taona, tikadzalowa m'dzikomo ife, uzimanga cingwe ici cofiira pazenera pamene watitsitsira; ndipo udzasonkhanitsa m'nyumbamo atate wako ndi mai wako nui abale ako ndi a m'nyumba onse a atate wako.

19. Ndipo kudzakhala kuti ali yense akadzaturuka pa khomo la nyumba yako kubwalo, imfa imeneyi ndi yace, tiribe kuparamula ife; koma ali yense adzakhala ndi iwe m'nyumba, likamfikira dzanja, imfa imeneyi ndi yathu.

20. Koma ukaulula codzera ifeco tidzamasukira lumbiro lako watilumbiritsali.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 2