Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 2:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo amunawo anati kwa iye, Moyo wathu ndiwo moyo wanu, mukapanda kuulula codzera ife; ndipo kudzakhala kuti, pakutipatsa ife dziko ili Yehova, tidzakucitira cifundo ndi coonadi.

15. Pamenepo anawatsitsa pazenera ndi cingwe; popeza nyumba yace lnali pa linga La mudzi, nakhala iye palingapo.

16. Ndipo anati kwa iwo, Mukani kuphiri, olondola angakupezeni; mubisale kumeneko masiku atatu, mpaka atabwerera olondolawo, pamenepo muyende ulendo wanu.

17. Ndipo amunawo anati kwa iye, Sitidzacimwira lumbiro lako ili watilumbiritsali.

18. Taona, tikadzalowa m'dzikomo ife, uzimanga cingwe ici cofiira pazenera pamene watitsitsira; ndipo udzasonkhanitsa m'nyumbamo atate wako ndi mai wako nui abale ako ndi a m'nyumba onse a atate wako.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 2