15. Momwemo ananyamula Yona, namponya m'nyanja; ndipo nyanja inaleka kukokoma kwace.
16. Ndipo amunawo anaopa Yehova ndi manthaakuru, namphera Yehova nsembe, nawinda.
17. Koma Yehova anaikiratu cinsomba cacikuru cimeze Yona; ndipo Yona anali m'miroba mwa nsombayi masiku atatu usana ndi usiku.