Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 9:8-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Woyala thambo yekha,Naponda pa mafunde a panyanja.

9. Wolenga Mlalang'amba, Akamwiniatsatana, ndi Nsangwe,Ndi Kumpotosimpita,

10. Wocita zazikuru zosasanthulika,Ndi zodabwiza zosawerengeka,

11. Taona, Mulungu apita pali ine, koma sindimpenya;Napitirira, koma osamaindikira ine.

12. Taona, akwatula, adzambwezetsa ndani?Adzanena naye ndani, Mulikucita ciani?

13. Mulungu sadzabweza mkwiyo wace;Athandizi odzikuza awerama pansi pa Iye.

14. Nanga ine tsono ndidzamyankha bwanji,Ndi kusankha mau anga akutsutsana ndi Iye?

15. Ameneyo, cinkana ndikadakhala wolungama, sindikadamyankha; Ndikadangompembedza wondiweruza ine.

16. Ndikadaitana, ndipo akadayankha Iye,Koma sindikadakhulupirira kuti Iye wamvera mau anga,

17. Pakuti andityola ndi mkuntho,Nacurukitsa mabala anga kopanda cifukwa.

18. Sandilola kuti ndipume,Koma andidzaza ndi zowawa.

Werengani mutu wathunthu Yobu 9