24. Dziko lapansi laperekedwa m'dzanja la woipa;Aphimba maso a oweruza ace.Ngati sindiye, pali yaninso?
25. Tsopano masiku anga afulumira kuposa wamtokoma;Athawa osaona cokoma.
26. Apitirira ngati zombo zaliwiro;Ngati mphungu igudukira cakudya cace.
27. Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa,Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;
28. Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse,Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.
29. Mlandu udzanditsutsa;Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?
30. Ndikasamba madzi a cipale cofewaNdi kuyeretsa manja anga ndi sopo;
31. Mudzandibviikanso muli zoola,Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.