Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 9:24-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Dziko lapansi laperekedwa m'dzanja la woipa;Aphimba maso a oweruza ace.Ngati sindiye, pali yaninso?

25. Tsopano masiku anga afulumira kuposa wamtokoma;Athawa osaona cokoma.

26. Apitirira ngati zombo zaliwiro;Ngati mphungu igudukira cakudya cace.

27. Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa,Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;

28. Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse,Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.

29. Mlandu udzanditsutsa;Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?

30. Ndikasamba madzi a cipale cofewaNdi kuyeretsa manja anga ndi sopo;

31. Mudzandibviikanso muli zoola,Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.

Werengani mutu wathunthu Yobu 9