Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 9:11-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Taona, Mulungu apita pali ine, koma sindimpenya;Napitirira, koma osamaindikira ine.

12. Taona, akwatula, adzambwezetsa ndani?Adzanena naye ndani, Mulikucita ciani?

13. Mulungu sadzabweza mkwiyo wace;Athandizi odzikuza awerama pansi pa Iye.

14. Nanga ine tsono ndidzamyankha bwanji,Ndi kusankha mau anga akutsutsana ndi Iye?

15. Ameneyo, cinkana ndikadakhala wolungama, sindikadamyankha; Ndikadangompembedza wondiweruza ine.

16. Ndikadaitana, ndipo akadayankha Iye,Koma sindikadakhulupirira kuti Iye wamvera mau anga,

17. Pakuti andityola ndi mkuntho,Nacurukitsa mabala anga kopanda cifukwa.

18. Sandilola kuti ndipume,Koma andidzaza ndi zowawa.

19. Tikanena za mphamvu, si ndiye wamphamvu?Tikanena za kuweruza, adzamuitana ndani?

20. Cinkana ndikhala wolungama, pakamwa panga padzanditsutsa;Cinkana ndikhala wangwiro, padzanditsutsa wamphulupulu.

21. Cinkana ndikhala wangwiro, sindidzisamalira mwini,Ndipeputsa moyo wanga.

22. Kuli cimodzimodzi monsemo, m'mwemo ndikutiIye aononga wangwiro ndi woipa pamodzi.

23. Mkwapulo ukapha modzidzimutsa,Adzaseka tsoka la wosacimwa.

Werengani mutu wathunthu Yobu 9