Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 8:5-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Koma ukafunitsitsa Mulungu,Ndi kupembedza Wamphamvuyonse;

6. Ukakhala woyera ndi woongoka mtima,Zoonadi adzakugalamukira tsopano,Ndi kupindulitsa pokhala pako polungama.

7. Ndipo cinkana ciyambi cako cinali cacing'ono,Citsiriziro cako cidzacuruka kwambiri.

8. Pakuti ufunsire tsono mbadwo wapitawo,Nusamalire zimene makolo ao adazisanthula;

9. Pakuti ife ndife adzulo, osadziwa kanthu,Popeza masiku athu a pa dziko lapansi ndiwo ngati mthunzi;

10. Amene aja sangakuphunzitse, ndi kukufotokozera,Ndi kuturutsa mau a mumtima mwao?

11. Ngati gumbwa aphuka popanda cinyontho?Ngati mancedza amera popanda madzi?

12. Akali auwisi, sanawaceka,Auma, asanaume mathengo onse ena.

13. Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu;Ndi ciyembekezo ca onyoza Mulungu cidzatayika;

14. Kulimbika mtima kwace kudzatyoka,Cikhulupiriro cace cikunga nyumba ya tandaude.

15. Adzatsamira nyumba yace, koma yosamlimbira;Adzaiumirira koma yosakhalitsa.

16. Akhala wamuwisi pali dzuwa,Ndi nthambi zace ziturukira pamunda pace.

Werengani mutu wathunthu Yobu 8