Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 8:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Cinkana ana ako anamcimwira Iye,Ndipo anawapereka mwa kulakwa kwao;

5. Koma ukafunitsitsa Mulungu,Ndi kupembedza Wamphamvuyonse;

6. Ukakhala woyera ndi woongoka mtima,Zoonadi adzakugalamukira tsopano,Ndi kupindulitsa pokhala pako polungama.

7. Ndipo cinkana ciyambi cako cinali cacing'ono,Citsiriziro cako cidzacuruka kwambiri.

8. Pakuti ufunsire tsono mbadwo wapitawo,Nusamalire zimene makolo ao adazisanthula;

9. Pakuti ife ndife adzulo, osadziwa kanthu,Popeza masiku athu a pa dziko lapansi ndiwo ngati mthunzi;

10. Amene aja sangakuphunzitse, ndi kukufotokozera,Ndi kuturutsa mau a mumtima mwao?

11. Ngati gumbwa aphuka popanda cinyontho?Ngati mancedza amera popanda madzi?

12. Akali auwisi, sanawaceka,Auma, asanaume mathengo onse ena.

13. Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu;Ndi ciyembekezo ca onyoza Mulungu cidzatayika;

Werengani mutu wathunthu Yobu 8