Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 8:12-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Akali auwisi, sanawaceka,Auma, asanaume mathengo onse ena.

13. Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu;Ndi ciyembekezo ca onyoza Mulungu cidzatayika;

14. Kulimbika mtima kwace kudzatyoka,Cikhulupiriro cace cikunga nyumba ya tandaude.

15. Adzatsamira nyumba yace, koma yosamlimbira;Adzaiumirira koma yosakhalitsa.

16. Akhala wamuwisi pali dzuwa,Ndi nthambi zace ziturukira pamunda pace.

17. Mizu yace iyangayanga pa kasupe wamadzi,Apenyerera pokhalapo miyala.

18. Akamuononga kumcotsa pamalo pace,Padzamkana, ndi kuti, Sindinakuona.

19. Taona, ici ndico comkondweretsa panjira pace,Ndi panthaka padzamera ena.

20. Taona, Mulungu sakana munthu wangwiro;Kapena kugwiriziza ocita zoipa.

21. Koma adzadzaza m'kamwa mwako ndi kuseka,Ndi milomo yako kupfuula.

22. Iwo akudana nawe adzabvala manyazi;Ndi hema wa oipa adzakhala kuli zi.

Werengani mutu wathunthu Yobu 8