1. Pamenepo anayankha Bilidadi Msuki, nati,
2. Udzanena izi kufikira liti?Ndipo mau a pakamwa pako adzakhala ngati namondwe kufikira liti?
3. Ngati Mulungu akhotetsa ciweruzo?Ngati Wamphamvuyonse akhotetsa mlandu?
4. Cinkana ana ako anamcimwira Iye,Ndipo anawapereka mwa kulakwa kwao;
5. Koma ukafunitsitsa Mulungu,Ndi kupembedza Wamphamvuyonse;
6. Ukakhala woyera ndi woongoka mtima,Zoonadi adzakugalamukira tsopano,Ndi kupindulitsa pokhala pako polungama.
7. Ndipo cinkana ciyambi cako cinali cacing'ono,Citsiriziro cako cidzacuruka kwambiri.