Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 8:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo anayankha Bilidadi Msuki, nati,

2. Udzanena izi kufikira liti?Ndipo mau a pakamwa pako adzakhala ngati namondwe kufikira liti?

3. Ngati Mulungu akhotetsa ciweruzo?Ngati Wamphamvuyonse akhotetsa mlandu?

4. Cinkana ana ako anamcimwira Iye,Ndipo anawapereka mwa kulakwa kwao;

5. Koma ukafunitsitsa Mulungu,Ndi kupembedza Wamphamvuyonse;

6. Ukakhala woyera ndi woongoka mtima,Zoonadi adzakugalamukira tsopano,Ndi kupindulitsa pokhala pako polungama.

Werengani mutu wathunthu Yobu 8