Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 7:6-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Masiku anga afulumira koposa mphindo ya muomba,Apitirira opanda ciyembekezo.

7. Kumbukila kuti moyo wanga ndiwo mphepo,Diso langa silidzaonanso cokoma.

8. Diso la amene andiona silidzandionanso,Maso ako adzandipenyetsetsa, koma ine palibe.

9. Mtambo wapita watha,Momwemo wakutsikira kumanda sadzakwerakonso.

10. Sadzabweranso ku nyumba yace,Osamdziwanso malo ace.

11. Potero sindidzaletsa pakamwa panga;Ndidzalankhula popsinjika mumzimu mwanga;Ndidzadandaula pakuwawa mtima wanga.

12. Ndine nyanja kodi, kapena cinjoka ca m'nyanja,Kuti Inu mundiikira odikira?

13. Ndikati, Pakama panga mpondisangalatsa,Pogona panga padzacepsa condidandaulitsa;

14. Pamenepo mundiopsa ndi maloto,Nimundicititsa mantha ndi masomphenya;

15. Potero moyo wanga usankha kupotedwa,Ndi imfa, koposa mafupa anga awa.

16. Ndinyansidwa nao moyo wanga; sindidzakhala ndi moyo cikhalire;Mundileke; pakuti masiku anga ndi acabe.

17. Munthu ndani kuti mumkuze,Ndi kuti muike mtima wanu pa iye,

18. Ndi kuti muceze naye m'mawa ndi m'mawa,Ndi kumuyesa nthawi zonse?

Werengani mutu wathunthu Yobu 7