Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 7:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndine nyanja kodi, kapena cinjoka ca m'nyanja,Kuti Inu mundiikira odikira?

13. Ndikati, Pakama panga mpondisangalatsa,Pogona panga padzacepsa condidandaulitsa;

14. Pamenepo mundiopsa ndi maloto,Nimundicititsa mantha ndi masomphenya;

15. Potero moyo wanga usankha kupotedwa,Ndi imfa, koposa mafupa anga awa.

16. Ndinyansidwa nao moyo wanga; sindidzakhala ndi moyo cikhalire;Mundileke; pakuti masiku anga ndi acabe.

17. Munthu ndani kuti mumkuze,Ndi kuti muike mtima wanu pa iye,

Werengani mutu wathunthu Yobu 7