12. Ndine nyanja kodi, kapena cinjoka ca m'nyanja,Kuti Inu mundiikira odikira?
13. Ndikati, Pakama panga mpondisangalatsa,Pogona panga padzacepsa condidandaulitsa;
14. Pamenepo mundiopsa ndi maloto,Nimundicititsa mantha ndi masomphenya;
15. Potero moyo wanga usankha kupotedwa,Ndi imfa, koposa mafupa anga awa.
16. Ndinyansidwa nao moyo wanga; sindidzakhala ndi moyo cikhalire;Mundileke; pakuti masiku anga ndi acabe.
17. Munthu ndani kuti mumkuze,Ndi kuti muike mtima wanu pa iye,