Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 7:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kodi munthu alibe nkhondo kunja kuno?Kodi masiku ace sakunga masiku a wolembedwa nchito?

2. Monga kapolo woliralira mthunzi,Monga wolembedwa nchito ayembekezera mphotho yace,

3. Momwemo anandilowetsa miyezi yopanda pace.Nandiikiratu zowawa usiku ndi usiku.

4. Ndigona pansi, ndikuti,Ndidzauka liti? koma usiku undikulira;Ndipo ndimapalapata mpaka mbanda kuca.

5. Mnofu wanga wabvala mphutsi ndi nkanambo zadothi;Khungu langa lang'ambika, nilinyansa.

Werengani mutu wathunthu Yobu 7