Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 6:5-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?

6. Kodi cinthu cosakolera cidyeka copanda mcere?Coyera ca dzira cikolera kodi?

7. Zimene moyo wanga ukana kuzikhudzaZikunga cakudya cosakolera kwa ine.

8. Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!

9. Cimkomere Mulungu kundiphwanya,Alole dzanja lace lindilikhel

10. Pamenepo ndidzasangalala,Ndidzakondwera naco cowawa cosandileka;Pakuti sindinawabisa mau a Woyerayo.

11. Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze?Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?

12. Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala?Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?

13. Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.

14. Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo;Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.

15. Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje,Ngati madzi a timitsinje akupitirira.

16. Amada cifukwa ca madzi oundana.M'menemo cipale cofewa cibisika;

17. Atafikira mafundi, mitsinje iuma;Kukatentha, imwerera m'malo mwao.

18. Aulendo akutsata njira yao apambukapo,Akwerera poti se, natayika.

19. Aulendo a ku Tema anapenyerera,Makamu a ku Seba anaiyembekezera.

Werengani mutu wathunthu Yobu 6