Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 6:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti mibvi ya Wamphamvuyonse yandilowa,Mzimu wanga uumwa ulembe wace;Zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.

5. Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?

6. Kodi cinthu cosakolera cidyeka copanda mcere?Coyera ca dzira cikolera kodi?

7. Zimene moyo wanga ukana kuzikhudzaZikunga cakudya cosakolera kwa ine.

8. Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha,Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!

Werengani mutu wathunthu Yobu 6