23. Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani?Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?
24. Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine;Mundizindikiritse umo ndinalakwira.
25. Mau oongoka si ndiwo amphamvu?Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?
26. Kodi muyesa kudzudzula mau?Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.
27. Indetu, mugwetsera wamasiye msampha,Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.