Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 6:22-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ngati ndinati, Mundipatse?Kapena, Muperekeko kwa ine cuma canu?

23. Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani?Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?

24. Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine;Mundizindikiritse umo ndinalakwira.

25. Mau oongoka si ndiwo amphamvu?Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?

26. Kodi muyesa kudzudzula mau?Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.

27. Indetu, mugwetsera wamasiye msampha,Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.

28. Koma tsopano balindani, mundipenyerere;Ndikanena bodza pamaso panu mudzalizindikira.

29. Bwererani, ndikupemphani, musandiipsire mlandu;Inde, bwereraninso, mlandu wanga ngwolungama.

30. Kodi pali cosalungama palilime panga?Ngati sindizindikira zopanda pace m'kamwa mwanga?

Werengani mutu wathunthu Yobu 6