Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 6:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Anazimidwa popeza adaikhulupirira;Anafikako, nathedwa nzeru.

21. Pakuti tsopano mukhala mamwemo;Muona coopsa, mucitapo mantha.

22. Ngati ndinati, Mundipatse?Kapena, Muperekeko kwa ine cuma canu?

23. Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani?Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?

24. Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine;Mundizindikiritse umo ndinalakwira.

25. Mau oongoka si ndiwo amphamvu?Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?

26. Kodi muyesa kudzudzula mau?Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.

27. Indetu, mugwetsera wamasiye msampha,Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.

Werengani mutu wathunthu Yobu 6