15. Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje,Ngati madzi a timitsinje akupitirira.
16. Amada cifukwa ca madzi oundana.M'menemo cipale cofewa cibisika;
17. Atafikira mafundi, mitsinje iuma;Kukatentha, imwerera m'malo mwao.
18. Aulendo akutsata njira yao apambukapo,Akwerera poti se, natayika.
19. Aulendo a ku Tema anapenyerera,Makamu a ku Seba anaiyembekezera.
20. Anazimidwa popeza adaikhulupirira;Anafikako, nathedwa nzeru.
21. Pakuti tsopano mukhala mamwemo;Muona coopsa, mucitapo mantha.
22. Ngati ndinati, Mundipatse?Kapena, Muperekeko kwa ine cuma canu?
23. Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani?Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?
24. Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine;Mundizindikiritse umo ndinalakwira.
25. Mau oongoka si ndiwo amphamvu?Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?
26. Kodi muyesa kudzudzula mau?Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.
27. Indetu, mugwetsera wamasiye msampha,Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.
28. Koma tsopano balindani, mundipenyerere;Ndikanena bodza pamaso panu mudzalizindikira.
29. Bwererani, ndikupemphani, musandiipsire mlandu;Inde, bwereraninso, mlandu wanga ngwolungama.
30. Kodi pali cosalungama palilime panga?Ngati sindizindikira zopanda pace m'kamwa mwanga?