13. Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.
14. Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo;Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.
15. Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje,Ngati madzi a timitsinje akupitirira.
16. Amada cifukwa ca madzi oundana.M'menemo cipale cofewa cibisika;
17. Atafikira mafundi, mitsinje iuma;Kukatentha, imwerera m'malo mwao.
18. Aulendo akutsata njira yao apambukapo,Akwerera poti se, natayika.
19. Aulendo a ku Tema anapenyerera,Makamu a ku Seba anaiyembekezera.