Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 6:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma Yobu anayankha, nati,

2. Mwenzi atayesa bwino cisoni canga,Ndi kuika matsoka anga pamodzi pamuyeso!

3. Pakuti zikadalemera tsopano koposa mcenga wa kunyanja;Cifukwa cace mau anga ndasonthokera kunena.

4. Pakuti mibvi ya Wamphamvuyonse yandilowa,Mzimu wanga uumwa ulembe wace;Zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.

5. Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?

Werengani mutu wathunthu Yobu 6