1. Koma Yobu anayankha, nati,
2. Mwenzi atayesa bwino cisoni canga,Ndi kuika matsoka anga pamodzi pamuyeso!
3. Pakuti zikadalemera tsopano koposa mcenga wa kunyanja;Cifukwa cace mau anga ndasonthokera kunena.
4. Pakuti mibvi ya Wamphamvuyonse yandilowa,Mzimu wanga uumwa ulembe wace;Zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.
5. Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu?Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?